Anjatidwa Kaamba kodyesa Manyi Amzake

Eliza Bonongwe
0

 

Samuel Maonga



Apolisi ku Ntcheu dzulo amanga a Samuel Maonga a zaka 24 powaganizira kuti anakakamiza ana awiri kuchotsa chimbudzi chawo pogwiritsa ntchito kamwa.


Mneneri wa polisi ya Ntcheu Inspector Jacob Khembo wati, a Maonga anapeza ana awiriwa omwe ndi a zaka 9 ndi 11 akuzithandiza m'munda wawo wosalimidwa ndipo anawakakamiza kuti achotse chimbudzicho pogwiritsa ntchito kamwa.


Iwo ati makolo a anawa anadabwa kuwona kuti anawa amakanika kudya chakudya kunyumba ndipo atawafunsa anaulura zomwe anawachita a Maonga.


Makolo anawatengera anawa kuchipatala Cha Biliwiri komwe anawapasa uphungu wam'malingaliro ndipo kenako anakayitula nkhaniyi kupolisi.


A Samuel Maonga omwe amachokera m'mudzi mwa mwa Maonga dera la mfumu yaikulu Njolomole, akuyembekezeka kuyankha mlandu wodyetsa ana zinthu zoyipa.


Credit : Zodiak

Post a Comment

0 Comments
Post a Comment (0)
To Top